[1] Ndidzakukwezani Mulungu wanga, Mfumu yanga; ndidzatamanda dzina lanu ku nthawi za nthawi. [2] Ndidzakutamandani tsiku ndi tsiku ndi kulemekeza dzina lanu ku nthawi za nthawi. [3] Yehova ndi wamkulu ndi woyenera matamando onse; ukulu wake palibe angawumvetsetse. [4] Mʼbado wina udzayamikira ntchito yanu kwa mʼbado wina; Iwo adzafotokoza za machitidwe anu amphamvu. [5] Adzayankhula ulemerero wokongola waufumu wanu, ndipo ine ndidzalingalira za ntchito zanu zodabwitsa. [6] Iwo adzafotokoza za mphamvu ya ntchito zanu zoopsa kwambiri, ndipo ine ndidzalengeza za ntchito zanu zazikulu. [7] Adzakondwerera kuchuluka kwa ubwino wanu, ndi kuyimba mwachimwemwe za chilungamo chanu. [8] Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo, wosakwiya msanga ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika. [9] Yehova ndi wabwino kwa onse; amachitira chifundo zonse zimene anazipanga. [10] Zonse zimene munazipanga zidzakutamandani, Inu Yehova; oyera mtima adzakulemekezani. [11] Iwo adzafotokoza za ulemerero wa ufumu wanu ndi kuyankhula za mphamvu yanu, [12] kuti anthu onse adziwe za machitidwe anu amphamvu ndi ulemerero wokongola wa ufumu wanu. [13] Ufumu wanu ndi ufumu wamuyaya, ndipo ulamuliro wanu ndi wosatha pa mibado yonse. Yehova ndi wokhulupirika pa malonjezo ake onse ndi wokonda zonse zimene Iye anazipanga. [14] Yehova amagwiriziza onse amene akugwa ndipo amakweza onse otsitsidwa. [15] Maso a onse amayangʼana kwa Inu, ndipo Inu mumawapatsa chakudya chawo pa nthawi yoyenera. [16] Mumatsekula dzanja lanu ndi kukwaniritsa zokhumba za chamoyo chilichonse. [17] Yehova ndi wolungama mʼnjira zake zonse, ndi wokonda zonse zimene anazipanga. [18] Yehova ali pafupi ndi onse amene amamuyitana, onse amene amamuyitana Iye mʼchoonadi. [19] Iye amakwaniritsa zokhumba za iwo amene amamuopa; amamva kulira kwawo ndi kuwapulumutsa. [20] Yehova amayangʼana onse amene amamukonda koma adzawononga anthu onse oyipa. [21] Pakamwa panga padzayankhula zotamanda Yehova. Cholengedwa chilichonse chitamande dzina lake loyera ku nthawi za nthawi.