[1] Inu Yehova, kumbukirani Davide ndi mavuto onse anapirira. [2] Iye analumbira kwa Yehova ndi kulonjeza kwa Wamphamvu wa Yakobo kuti, [3] “Sindidzalowa mʼnyumba mwanga kapena kugona pa bedi langa: [4] sindidzalola kuti maso anga agone, kapena zikope zanga ziwodzere, [5] mpaka nditamupezera malo Yehova, malo okhala a Wamphamvu wa Yakobo.” [6] Zoonadi, tinamva za Bokosi la Chipangano ku Efurata, tinalipeza mʼminda ya ku Yaara: [7] “Tiyeni tipite ku malo ake okhalamo; tiyeni tikamulambire pa mapazi ake. [8] ‘Dzukani Yehova, ndipo bwerani ku malo anu opumulira, Inuyo ndi Bokosi la Chipangano limene limafanizira mphamvu zanu. [9] Ansembe anu avekedwe chilungamo; anthu anu oyera mtima ayimbe nyimbo mwachimwemwe.’ ” [10] Chifukwa cha Davide mtumiki wanu, musakane wodzozedwa wanu. [11] Yehova analumbira kwa Davide, lumbiro lotsimikizika kuti Iye sadzasintha: “Mmodzi wa ana ako ndidzamuyika pa mpando waufumu; [12] ngati ana ako azisunga pangano langa ndi malamulo amene ndiwaphunzitsa, pamenepo ana awo adzakhala pa mpando wako waufumu kwamuyaya ndi muyaya.” [13] Pakuti Yehova wasankha Ziyoni, Iye wakhumba kuti akhale malo ake okhalamo: [14] “Awa ndi malo anga opumapo ku nthawi za nthawi; ndidzakhala pano pa mpando waufumu, pakuti ndakhumba zimenezi. [15] Ndidzadalitsa mzindawu ndi zinthu zambiri; anthu ake osauka ndidzawakhutitsa ndi chakudya. [16] Ndidzaveka ansembe ake chipulumutso, ndipo anthu ake oyera mtima adzayimba nthawi zonse nyimbo zachimwemwe. [17] “Pano ndidzachulukitsa mphamvu za Davide ndi kuyikapo nyale ya wodzozedwa wanga. [18] Ndidzaveka adani ake manyazi, koma chipewa chaufumu pamutu pake chidzakhala chowala.”