[1] Akanapanda kukhala mbali yathu Yehova, anene tsono Israeli,
[2] akanapanda kukhala mbali yathu Yehova, potiwukira anthuwo,
[3] iwo atatipsera mtima, akanatimeza amoyo;
[4] chigumula chikanatimiza, mtsinje ukanatikokolola,
[5] madzi a mkokomo akanatikokolola.
[6] Atamandike Yehova, amene sanalole kuti tikhale chakudya cha mano awo.
[7] Moyo wathu wawonjoka ngati mbalame yokodwa mu msampha wa mlenje; msampha wathyoka, ndipo ife tapulumuka.
[8] Thandizo lathu lili mʼdzina la Yehova wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.