Masalimo 124:1-8 OCCL

[1] Akanapanda kukhala mbali yathu Yehova, anene tsono Israeli, [2] akanapanda kukhala mbali yathu Yehova, potiwukira anthuwo, [3] iwo atatipsera mtima, akanatimeza amoyo; [4] chigumula chikanatimiza, mtsinje ukanatikokolola, [5] madzi a mkokomo akanatikokolola. [6] Atamandike Yehova, amene sanalole kuti tikhale chakudya cha mano awo. [7] Moyo wathu wawonjoka ngati mbalame yokodwa mu msampha wa mlenje; msampha wathyoka, ndipo ife tapulumuka. [8] Thandizo lathu lili mʼdzina la Yehova wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.