Masalimo 124:1-8 OCCL

[1] Akanapanda kukhala mbali yathu Yehova, anene tsono Israeli, [2] akanapanda kukhala mbali yathu Yehova, potiwukira anthuwo, [3] iwo atatipsera mtima, akanatimeza amoyo; [4] chigumula chikanatimiza, mtsinje ukanatikokolola, [5] madzi a mkokomo akanatikokolola. [6] Atamandike Yehova, amene sanalole kuti tikhale chakudya cha mano awo. [7] Moyo wathu wawonjoka ngati mbalame yokodwa mu msampha wa mlenje; msampha wathyoka, ndipo ife tapulumuka. [8] Thandizo lathu lili mʼdzina la Yehova wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app ★★★★★4.8 · 216K ratings Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.