[1] Tamandani Yehova. Ndidzathokoza Yehova ndi mtima wanga wonse mʼbwalo la anthu olungama mtima ndi pa msonkhano. [2] Ntchito za Yehova nʼzazikulu; onse amene amakondwera nazo amazilingalira. [3] Zochita zake ndi za ulemerero ndi zaufumu, ndipo chilungamo chake ndi chosatha. [4] Iye wachititsa kuti zodabwitsa zake zikumbukirike; Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo. [5] Amapereka chakudya kwa amene amamuopa Iye; amakumbukira pangano lake kwamuyaya. [6] Waonetsa anthu ake mphamvu ya ntchito zake, kuwapatsa mayiko a anthu a mitundu ina. [7] Ntchito za manja ake ndi zokhulupirika ndi zolungama; malangizo ake onse ndi odalirika. [8] Malamulo ndi okhazikika ku nthawi za nthawi, ochitidwa mokhulupirika ndi molungama. [9] Iyeyo amawombola anthu ake; anakhazikitsa pangano lake kwamuyaya dzina lake ndi loyera ndi loopsa. [10] Kuopa Yehova ndicho chiyambi cha nzeru; onse amene amatsatira malangizo ake amamvetsa bwino zinthu. Iye ndi wotamandika mpaka muyaya.