Masalimo 109:1-31 OCCL
[1] Mulungu amene ndimakutamandani, musakhale chete, [2] pakuti anthu oyipa ndi achinyengo atsekula pakamwa pawo kutsutsana nane; iwo ayankhula motsutsana nane ndi malilime abodza. [3] Andizungulira ndi mawu audani, amandinena popanda chifukwa. [4] Mʼmalo mwa chikondi changa amandineneza, koma ine ndine munthu wapemphero. [5] Iwo amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino, ndi udani mʼmalo mwa chikondi changa. [6] Sankhani munthu woyipa kuti amutsutse iye; lolani wotsutsa ayime ku dzanja lake lamanja. [7] Pamene aweruzidwa, apezeke kuti ndi wolakwa, ndipo mapemphero ake amutsutse. [8] Masiku ake akhale owerengeka; munthu wina atenge malo ake a utsogoleri. [9] Ana ake akhale amasiye ndipo mkazi wake akhale wopanda mwamuna. [10] Ana ake akhale oyendayenda ndi opemphapempha; apirikitsidwe kuchoka pa mabwinja a nyumba zawo. [11] Wokongoza alande zonse zimene ali nazo; alendo afunkhe ntchito za manja ake. [12] Pasapezeke ndi mmodzi yemwe womukomera mtima kapena kumvera chisoni ana ake amasiye. [13] Zidzukulu zake zithe nʼkufa, mayina awo afafanizidwe mu mʼbado wotsatirawo. [14] Mphulupulu za makolo ake zikumbukiridwe pamaso pa Yehova; tchimo la amayi ake lisadzafafanizidwe. [15] Machimo awo akhale pamaso pa Yehova nthawi zonse, kuti Iye achotse chikumbutso chawo pa dziko lapansi. [16] Pakuti iye sanaganizirepo zochita chifundo, koma anazunza mpaka kuwapha anthu osauka ndi osweka mtima. [17] Anakonda kutemberera, matembererowo abwerere kwa iye; sanakondwe nʼkudalitsa anthu ena, choncho madalitso akhale kutali naye. [18] Anavala kutemberera ngati chovala; kutemberera kunalowa mʼthupi lake ngati madzi, kulowa mʼmafupa ake ngati mafuta. [19] Matemberero akhale ngati chofunda chodzikutira nacho, ngati lamba wovala tsiku ndi tsiku. [20] Awa akhale malipiro ochokera kwa Yehova pa onditsutsa anga, kwa iwo amene amayankhula zoyipa za ine. [21] Koma Inu Ambuye Wamphamvuzonse, muchite nane molingana ndi dzina lanu, chifukwa cha ubwino wa chikondi chanu, pulumutseni. [22] Pakuti ndine wosauka ndi wosowa, ndipo mtima wanga ukuwawa mʼkati mwanga. [23] Ndikuzimirira ngati mthunzi wa kumadzulo, ndapirikitsidwa ngati dzombe. [24] Mawondo anga afowoka chifukwa cha kusala zakudya, thupi langa lawonda ndi mutu wanga womwe. [25] Ndine chinthu chotonzedwa kwa otsutsana nane; akandiona, amapukusa mitu yawo. [26] Thandizeni Inu Yehova Mulungu wanga; pulumutseni molingana ndi chikondi chanu. [27] Adaniwo adziwe kuti limeneli ndi dzanja lanu, kuti Inu Yehova mwachita zimenezi. [28] Angathe kutemberera, koma Inu mudzadalitsa; pamene iwo andiputa adzachititsidwa manyazi, koma mtumiki wanu adzasangalala. [29] Onditsutsa adzavekedwa mnyozo, ndipo adzadzifunditsa manyazi ngati chovala. [30] Ndi pakamwa panga ndidzathokoza Yehova kwambiri; ndidzamutamanda mʼgulu lalikulu la anthu. [31] Popeza Iye amayima ku dzanja lamanja la munthu wosowayo, kupulumutsa moyo wake kwa iwo amene agamula molakwa.
