Masalimo 100:1-5 OCCL

[1] Fuwulani kwa Yehova mwachimwemwe, inu dziko lonse lapansi. [2] Mulambireni Yehova mosangalala; bwerani pamaso pake ndi nyimbo zachikondwerero. [3] Dziwani kuti Yehova ndi Mulungu. Iye ndiye amene anatipanga ndipo ife ndife ake; ndife anthu ake, nkhosa za pabusa pake. [4] Lowani ku zipata zake ndi chiyamiko ndi ku mabwalo ake ndi matamando; muyamikeni ndi kutamanda dzina lake. [5] Pakuti Yehova ndi wabwino ndipo chikondi chake ndi chamuyaya; kukhulupirika kwake nʼkokhazikika pa mibado ndi mibado.

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.