Maliro 3:1-66 OCCL
[1] Ine ndine munthu amene ndaona masautso ndi ndodo ya ukali wake. [2] Wandipititsa kutali ndipo wandiyendetsa mu mdima osati mʼkuwala; [3] zoonadi anandikantha ndi dzanja lake mobwerezabwereza tsiku lonse. [4] Wakalambitsa khungu langa ndi mnofu wanga, ndipo waphwanya mafupa anga. [5] Wandizinga ndi kundizungulira ndi zowawa ndi zolemetsa. [6] Wandikhazika mu mdima ngati amene anafa kale. [7] Wandimangira khoma kotero kuti sindingathawe, wandimanga ndi maunyolo. [8] Ngakhale pamene ndifuwula kapena kupempha chithandizo, amakana pemphero langa. [9] Wanditsekera njira yanga ndi miyala yosema; ndipo wakhotetsa tinjira tanga. [10] Wandidikirira ngati chimbalangondo, wandibisalira ngati mkango. [11] Wandikokera pambali ndi kundingʼambangʼamba, ndipo wandisiya wopanda thandizo. [12] Wakoka uta wake ndipo walunjikitsa mivi yake pa ine. [13] Walasa mtima wanga ndi mivi ya mʼphodo mwake. [14] Ndinakhala choseketsa cha anthu anga onse; amandinyodola mʼnyimbo zawo tsiku lonse. [15] Wandidyetsa zowawa ndipo wandimwetsa ndulu. [16] Wathyola mano anga ndi miyala; wandiviviniza mʼfumbi; [17] Wandichotsera mtendere; ndayiwala kuti kupeza bwino nʼchiyani. [18] Choncho ndikuti, “Ulemerero wanga wachoka ndi zonse zimene ndimayembekeza kwa Yehova.” [19] Kukumbukira masautso anga ndi kusowa pokhala, zili ngati zowawa ndi ndulu. [20] Ine ndikuzikumbukira bwino izi, ndipo moyo wanga wathedwa mʼkati mwanga. [21] Komabe ndimakumbukira zimenezi, nʼchifukwa chake ndili ndi chiyembekezo. [22] Ife sitinawonongekeretu chifukwa chikondi cha Yehova ndi chachikulu, ndi chifundo chake ndi chosatha. [23] Zimaoneka zatsopano mmawa uliwonse; kukhulupirika kwanu nʼkwakukulu. [24] Mu mtima mwanga ndimati, “Yehova ndiye zanga zonse; motero ndimamuyembekezera.” [25] Yehova ndi wabwino kwa amene amayembekezera Iye, kwa munthu amene amafunafuna Iyeyo; [26] nʼkwabwino kudikira chipulumutso cha Yehova modekha. [27] Nʼkwabwino kuti munthu asenze goli pamene ali wamngʼono. [28] Akhale chete pa yekha, chifukwa Yehova wamusenzetsa golilo. [29] Abise nkhope yake mʼfumbi mwina chiyembekezo nʼkukhalapobe. [30] Apereke tsaya lake kwa iye amene angamumenye, ndipo amuchititse manyazi. [31] Chifukwa Ambuye satayiratu anthu nthawi zonse. [32] Ngakhale amabweretsa zowawa, Iye adzawachitira chifundo, chifukwa chikondi chake ndi chosatha. [33] Pakuti sabweretsa masautso mwadala, kapena zowawa kwa ana a anthu. [34] Kuphwanya ndi phazi a mʼndende onse a mʼdziko, [35] kukaniza munthu ufulu wake pamaso pa Wammwambamwamba, [36] kumana munthu chiweruzo cholungama—kodi Ambuye saona zonsezi? [37] Kodi ndani angayankhule zinthu nʼkuchitika ngati Ambuye sanavomereze? [38] Kodi zovuta ndi zabwino sizituluka mʼkamwa mwa Wammwambamwamba? [39] Kodi nʼchifukwa chiyani munthu aliyense wamoyo amadandaula akalangidwa chifukwa cha machimo ake? [40] Tiyeni tisanthule ndi kuyesa njira zathu, ndipo tiyeni tibwerere kwa Yehova. [41] Tiyeni tikweze mitima yathu ndi manja athu kwa Mulungu kumwamba ndipo tinene kuti: [42] “Ife tachimwa ndi kuwukira ndipo inu simunakhululuke. [43] “Mwadzikuta ndi mkwiyo ndi kutilondola ndipo mwatitha mopanda chifundo. [44] Mwadzikuta mu mtambo kotero mapemphero athu sakukufikani. [45] Mwatisandutsa zinyatsi ndi zinyalala pakati pa mitundu ya anthu. [46] “Adani anthu atitsekulira pakamwa. [47] Ife tadzazidwa ndi mantha pakuti tagwa mʼdzenje, tapasuka ndi kuwonongedwa.” [48] Misozi mʼmaso mwanga ikungoti mbwembwembwe chifukwa anthu anga akuwonongedwa. [49] Misozi idzatsika kosalekeza, ndipo sidzasiya, [50] mpaka Yehova ayangʼane pansi kuchokera kumwamba ndi kuona. [51] Mtima wanga ukupweteka poona zimenezi chifukwa cha akazi onse a mu mzinda. [52] Akundisaka ngati mbalame, amene anali adani anga, popanda chifukwa. [53] Ayesa kundipha pondiponya mʼdzenje ndi kundiponya miyala; [54] madzi anamiza mutu wanga ndipo ndinkaganiza kuti imfa yayandikira. [55] Ndinayitana dzina lanu Inu Yehova, kuchokera mʼdzenje lozama. [56] Inu munamva kudandaula kwanga. “Mundimvere kulira kwanga kopempha thandizo.” [57] Munafika pafupi pamene ndinakuyitanani, ndipo munati, “Usaope.” [58] Inu Ambuye munandiwombola ku mlandu wanga; munapulumutsa moyo wanga. [59] Yehova, mwaona zoyipa zimene andichitira. Mundiweruzire ndinu! [60] Mwaona kuzama kwa kubwezera kwawo, chiwembu chawo chonse pa ine. [61] Inu Yehova mwamva kunyoza kwawo, chiwembu chawo chonse pa ine, [62] manongʼonongʼo a adani anga ondiwukira ine tsiku lonse. [63] Tawaonani! Kaya ali pansi kapena kuyimirira, akundinyoza mu nyimbo zawo. [64] Inu Yehova, muwabwezere chowayenera, chifukwa cha zimene manja awo achita. [65] Phimbani mitima yawo, ndipo matemberero anu akhale pa iwo! [66] Muwalondole mwaukali ndipo muwawonongeretu pa dziko lapansi.
