Genesis 5:1-32 OCCL
[1] Ndondomeko ya mibado ya Adamu ndi iyi: Pamene Mulungu analenga munthu, anamulenga mʼchifaniziro cha Mulungu. [2] Iye analenga mwamuna ndi mkazi. Anawadalitsa ndipo anawatcha “Munthu.” [3] Pamene Adamu anali ndi zaka 130, anabereka mwana wamwamuna wofanana naye ndipo anamutcha Seti. [4] Atabadwa Seti, Adamu anakhala ndi moyo zaka zina 800 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi. [5] Zaka zonse za Adamu zinali 930 ndipo anamwalira. [6] Pamene Seti anali ndi zaka 105, anabereka Enosi. [7] Atabadwa Enosi, Seti anakhala ndi moyo zaka zina 807 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi. [8] Zaka zonse za Seti zinali 912 ndipo anamwalira. [9] Pamene Enosi anali ndi zaka 90, anabereka Kenani. [10] Atabadwa Kenani, Enosi anakhala ndi moyo zaka zina 815 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi. [11] Zaka zonse za Enosi pamodzi zinali 905 ndipo anamwalira. [12] Pamene Kenani anali ndi zaka 70, anabereka Mahalaleli. [13] Atabadwa Mahalaleli, Kenani anakhala ndi moyo zaka zina 840 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi. [14] Zaka zonse za Kenani zinali 910, ndipo anamwalira. [15] Pamene Mahalaleli anali ndi zaka 65, anabereka Yaredi. [16] Atabadwa Yaredi, Mahalaleli anakhala ndi moyo zaka zina 830 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi. [17] Zaka zonse za Mahalaleli zinali 895 ndipo anamwalira. [18] Pamene Yaredi anali ndi zaka 162, anabereka Enoki. [19] Atabadwa Enoki, Yaredi anakhala ndi moyo zaka zina 800 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi. [20] Zaka zonse za Yaredi zinali 962 ndipo anamwalira. [21] Pamene Enoki anali ndi zaka 65, anabereka Metusela. [22] Atabadwa Metusela, Enoki anayenda ndi Mulungu zaka 300 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi. [23] Zaka zonse za Enoki zinali 365. [24] Enoki anayenda ndi Mulungu; ndipo iye sanaonekenso chifukwa Mulungu anamutenga. [25] Pamene Metusela anali ndi zaka 187, anabereka Lameki. [26] Ndipo atabadwa Lameki, Metusela anakhala ndi moyo zaka zina 782 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi. [27] Zaka zonse za Metusela zinali 969, ndipo anamwalira. [28] Pamene Lameki anali ndi zaka 182, anabereka mwana wamwamuna. [29] Ndipo anamutcha Nowa ndipo anati, “Iyeyu adzatipumulitsa ku ntchito zathu zolemetsazi, zolima nthaka imene Yehova anayitemberera.” [30] Atabadwa Nowa, Lameki anakhala zaka zina 595 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi. [31] Zaka zonse za Lameki zinali 777, ndipo kenaka anamwalira. [32] Pamene Nowa anali ndi zaka 500, anabereka Semu, Hamu ndi Yafeti.
