Genesis 10:1-32 OCCL
[1] Nayi mbiri ya ana a Nowa, Semu, Hamu ndi Yafeti. Ana atatuwa anabereka ana awo chitatha chigumula. [2] Ana aamuna a Yafeti anali: Gomeri, Magogi, Madai, Yavani, Tubala, Mesaki ndi Tirasi. [3] Ana aamuna a Gomeri anali: Asikenazi, Rifati ndi Togarima. [4] Ana aamuna a Yavani anali: Elisa, Tarisisi, Kitimu ndi Rodanimu. [5] (Amenewa ndiwo makolo a anthu okhala mʼmphepete mwa nyanja. Awa ndi ana a Yafeti monga mwa mafuko a mu mitundu yawo, uliwonse ndi chiyankhulo chake). [6] Ana aamuna a Hamu anali: Kusi, Miziraimu, Puti ndi Kanaani. [7] Ana aamuna a Kusi anali: Seba, Havila, Sabita, Raama ndi Sabiteka. Ana aamuna a Raama anali: Seba ndi Dedani. [8] Kusi anabereka Nimurodi amene anali wankhondo wamphamvu kwambiri pa dziko lapansi. [9] Iye anali mlenje wamphamvu kwambiri pamaso pa Yehova; nʼchifukwa chake anthu ali ndi chisudzo, chakuti, “Ndiwe mlenje wamphamvu kwambiri pamaso pa Yehova monga Nimurodi.” [10] Malo oyambirira a ufumu wake anali Babeli, Ereki, Akadi ndi Kaline. Malo onsewa anali mʼdziko la Sinara. [11] Atachoka mʼdziko limeneli anapita ku Asiriya kumene anakamanga Ninive, Rehoboti-Iri, Kala, [12] ndi Reseni, mzinda waukulu umene uli pakati pa Ninive ndi Kala. [13] Igupto ndiye kholo la Aludi, Aanami, Alehabu, Anafutu, [14] Apaturusi, Akasilu ndi Akafitori (kumene kunachokera Afilisti). [15] Kanaani anabereka mwana wake wachisamba, Sidoni, ndipo anaberekanso Ahiti; [16] Ayebusi, Aamori, Agirigasi; [17] Ahivi, Aariki, Asini, [18] Aaravadi, Azemari ndi Ahamati. Pambuyo pake, mafuko a Akanaani anafalikira ponseponse, [19] mpaka ku malire a Kanaani. Malirewo anachokera ku Sidoni kulowa cha ku Gerari mpaka ku Gaza, ndi kulowa ku Sodomu, Gomora, Adima ndi Zeboimu mpaka ku Lasa. [20] Amenewa ndiwo ana aamuna a Hamu monga mwa mafuko ndi ziyankhulo zawo, mʼmadera omwe amakhala ndi mitundu yawo. [21] Semu amene anali mkulu wake wa Yafeti nayenso anabereka nakhala kholo la Eberi. [22] Ana aamuna a Semu anali: Elamu, Asuri, Aripakisadi, Ludi ndi Aramu. [23] Ana aamuna a Aramu anali: Uzi, Huri, Geteri ndi Mesaki. [24] Aripakisadi anabereka Sela, ndipo Selayo anabereka Eberi. [25] A Eberi anabereka ana aamuna awiri: Wina anamutcha Pelegi chifukwa pa nthawiyo anthu a pa dziko lapansi anagawikana. Dzina la mʼbale wake linali Yokitani. [26] Yokitani anabereka Alimodadi, Selefi, Hazari-Maveti, Yera, [27] Hadoramu, Uzali, Dikila, [28] Obali, Abimaeli, Seba, [29] Ofiri, Havila ndi Yobabu. Onsewa anali ana aamuna a Yokitani. [30] Chigawo chimene ankakhala chinayambira ku Mesa mpaka ku Seferi, ku dera la mapiri chakummawa. [31] Amenewa ndiwo ana a Semu monga mwa mafuko ndi ziyankhulo zawo, mʼmadera omwe ankakhala ndi mitundu yawo. [32] Amenewa ndiwo mafuko a ana aamuna a Nowa monga mwa mibado ya mitundu yawo. Mitundu yonse ya anthu inatuluka mwa iwowa ndi kufalikira pa dziko lonse lapansi chitatha chigumula chija.
