Eksodo 40:1-38 OCCL
[1] Kenaka Yehova anati kwa Mose, [2] “Imika chihema, tenti ya msonkhano, tsiku loyamba la mwezi. [3] Uyikemo bokosi la umboni ndipo uphimbe bokosilo ndi katani. [4] Ulowetsemo tebulo ndi kuyika zimene zimakhala pamenepo. Kenaka ulowetse choyikapo nyale ndipo uyikepo nyale zake. [5] Uyike guwa lofukiza la golide patsogolo pa bokosi la umboni ndipo uyike katani ya pa chipata cha chihema. [6] “Uyike guwa lansembe yopsereza patsogolo pa chipata cha chihema, tenti ya msonkhano. [7] Uyike beseni pakati pa tenti ya msonkhano ndi guwa lansembe ndipo uyikemo madzi. [8] Upange bwalo lozungulira chihemacho ndipo uyike katani ya pa chipata cha bwalolo. [9] “Utenge mafuta wodzozera ndipo udzoze chihema ndi chilichonse chili mʼmenemo ndipo zidzakhala zoyeretsedwa. [10] Kenaka udzoze guwa lansembe lopsereza ndi ziwiya zake zonse. Ulipatule guwalo ndipo lidzakhala loyera kwambiri. [11] Udzoze beseni ndi miyendo yake ndipo uzipatule. [12] “Ubwere ndi Aaroni ndi ana ake pa chipata cha tenti ya msonkhano ndipo uwasambitse ndi madzi. [13] Kenaka umuveke Aaroni zovala zopatulika, umudzoze ndi kumupatula kotero kuti athe kunditumikira monga wansembe. [14] Ubweretse ana ake ndipo uwaveke minjiro. [15] Uwadzoze monga momwe unadzozera abambo awo, kotero kuti anditumikire monga ansembe. Kudzozedwako kudzakhala unsembe wawo pa mibado ndi mibado” [16] Mose anachita zonse monga Yehova anamulamulira. [17] Kotero anayimika chihema tsiku loyamba la mwezi woyamba mʼchaka chachiwiri. [18] Nthawi imene Mose anayimika chihema, anayika matsinde mʼmalo ake, kuyimitsa maferemu, kulowetsa mitanda ndi kuyika nsichi. [19] Kenaka anayika tenti pamwamba pa chihema ndipo anayika chophimba pa tenti monga momwe Yehova analamulira Mose. [20] Iye anatenga miyala ya umboni nayika mʼbokosi lija ndi kuyika chivundikiro pamwamba pake. [21] Kenaka analowetsa bokosilo mʼchihema ndipo anapachika katani ndi kubisa bokosi la umboni monga momwe Yehova analamulira iye. [22] Mose anayika tebulo mu tenti ya msonkhano kumpoto kwa chihema, kunja kwa katani, [23] ndipo anayikapo buledi pamaso pa Yehova, monga momwe Yehova analamulira Mose. [24] Iye anayikanso choyikapo nyale mu tenti ya msonkhano moyangʼanana ndi tebulo mbali yakummwera kwa chihema. [25] Ndipo anayikapo nyale zija pamaso pa Yehova, monga Yehova analamulira Mose. [26] Mose anayika guwa la golide mu tenti ya msonkhano patsogolo pa katani [27] ndipo anapserezapo lubani wonunkhira monga Yehova anamulamulira. [28] Kenaka anayika katani ya pa chipata cha chihema. [29] Iye anayika guwa lansembe yopsereza pafupi ndi chipata cha chihema, tenti ya msonkhano, ndipo anapereka nsembe yopsereza ndi nsembe ya ufa monga Yehova anamulamulira. [30] Iye anayika beseni pakati pa tenti ya msonkhano ndi guwa lansembe ndipo anathiramo madzi wosamba, [31] ndipo Mose, Aaroni ndi ana ake amasamba manja ndi mapazi awo. [32] Iwo amasamba nthawi zonse akamalowa mu tenti ya msonkhano kapena kuyandikira guwa lansembe monga Yehova analamulira Mose. [33] Kenaka Mose anamanga bwalo kuzungulira chihema ndi guwa lansembe ndipo anayika katani ya pa chipata cha bwalo. Kotero Mose anamaliza ntchito. [34] Kenaka mtambo unaphimba tenti ya msonkhano, ndipo ulemerero wa Yehova unadzaza mʼchihemacho. [35] Mose sanathe kulowa mu tenti ya msonkhano chifukwa mtambo unali utakhazikika pa chihemacho, ndipo ulemerero wa Yehova unadzaza mʼchihemacho. [36] Pa maulendo awo onse, mtambo ukachoka pamwamba pa chihema, Aisraeli ankasamukanso pamene analipo. [37] Koma ngati mtambo sunachoke, iwo sankasamukanso mpaka tsiku limene udzachoke. [38] Kotero mtambo wa Yehova unkakhala pamwamba pa chihema usana, ndi mtambo wamoto umakhala usiku, pamaso pa nyumba yonse ya Israeli pa masiku onse aulendo wawo.
