Aefeso 5:1-33 OCCL
[1] Choncho, monga ana okondedwa, tsatirani chitsanzo cha Mulungu. [2] Muzikondana monga Khristu anakonda ife nadzipereka yekha chifukwa cha ife monga chopereka cha fungo lokoma ndi nsembe kwa Mulungu. [3] Koma pakati panu pasamveke nʼpangʼono pomwe zadama, kapena za mtundu wina uliwonse wa chodetsa, kapena za umbombo, chifukwa izi ndi zosayenera kwa anthu oyera a Mulungu. [4] Musamatukwane, kuyankhula zopusa kapena kunena nthabwala zopanda pake, zomwe ndi zosayenera, koma mʼmalo mwake muziyamika. [5] Dziwani ichi, palibe wadama, wochita zonyansa kapena waumbombo, munthu wotero ali ngati wopembedza mafano, amenewa alibe malo mu ufumu wa Khristu ndi Mulungu. [6] Musalole wina akunamizeni ndi mawu opanda pake, pakuti chifukwa cha zinthu ngati izi mkwiyo wa Mulungu ukubwera pa amene samvera. [7] Nʼchifukwa chake musamayanjane nawo anthu otere. [8] Pajatu inu nthawi ina munali mdima, koma tsopano ndinu kuwunika mwa Ambuye. Mukhale ngati ana akuwunika [9] (pakuti pamene pali kuwunika pamapezekaponso zabwino zonse, chilungamo ndi choonadi). [10] Inu mufufuze chimene chimakondweretsa Ambuye. [11] Musayanjane nazo ntchito zosapindulitsa za mdima, koma mʼmalo mwake muzitsutse. [12] Pakuti ndi zochititsa manyazi ngakhale kutchula zomwe zimachitika mseri. [13] Koma kuwala kumawunikira zinthu, ndipo chilichonse chimaonekera poyera. Choncho chilichonse choonekera poyera chimasandukanso kuwala. [14] Nʼchifukwa chake Malemba akuti, “Dzuka, wamtulo iwe, uka kwa akufa, ndipo Khristu adzakuwalira.” [15] Samalani makhalidwe anu, musakhale ngati opanda nzeru koma ngati anzeru. [16] Gwiritsani ntchito mpata uliwonse, chifukwa masiku ano ndi oyipa. [17] Choncho musakhale opusa, koma mudziwe zimene Ambuye akufuna kuti muchite. [18] Musaledzere ndi vinyo, chifukwa adzawononga moyo wanu. Mʼmalo mwake, mudzazidwe ndi Mzimu Woyera. [19] Muziyankhulana wina ndi mnzake mawu a Masalimo, nyimbo za Mulungu ndi nyimbo za uzimu. Muziyimbira Ambuye movomerezana ndi mitima yanu. [20] Muziyamika Mulungu Atate nthawi zonse chifukwa cha zonse, mʼdzina la Ambuye athu Yesu Khristu. [21] Gonjeranani wina ndi mnzake, kuonetsa kuopa Khristu. [22] Inu akazi, muzigonjera amuna anu, monga mumagonjera kwa Ambuye. [23] Pakuti mwamuna ndi mutu wa mkazi monga momwe Khristu ali mutu wa mpingo, thupi lake, limene Iyeyo ndi Mpulumutsi wake. [24] Tsono monga mpingo umagonjera Khristu, momwemonso akazi akuyenera kugonjera amuna awo mu zonse. [25] Inu amuna, kondani akazi anu monga momwe Khristu anakondera mpingo nadzipereka yekha mʼmalo mwa mpingowo [26] kuti awupatule ukhale oyera, atawuyeretsa powusambitsa ndi madzi omwe ndi mawu ake. [27] Anachita zimenezi kuti awupereke mpingowo kwa Iye mwini, mpingo wowala ndi waulemerero, wopanda banga kapena makwinya kapena chilema chilichonse, koma oyera ndi wangwiro. [28] Momwemonso, amuna akuyenera kukonda akazi awo monga matupi awo. Iye amene akonda mkazi wake adzikondanso yekha. [29] Pakuti palibe amene amadana nalo thupi lake, koma amalidyetsa ndi kulisamalira bwino, monga momwe Khristu amachitira ndi mpingo wake [30] pakuti ndife ziwalo za thupi lake. [31] “Pa chifukwa ichi, mwamuna adzasiya abambo ndi amayi ake nakaphatikana ndi mkazi wake, ndipo awiriwo adzakhala thupi limodzi.” [32] Ichi ndi chinsinsi chozama, koma ine ndikunena za Khristu ndi mpingo. [33] Chomwecho, aliyense mwa inu akuyenera kukonda mkazi wake monga adzikondera iye mwini, ndipo mkazi akuyenera kulemekeza mwamuna wake.
