2 Samueli 22:1-51 OCCL
[1] Davide anayimbira Yehova nyimbo iyi pamene Yehovayo anamupulumutsa mʼdzanja la adani ake onse ndiponso mʼdzanja la Sauli. [2] Iye anati, “Yehova ndiye thanthwe langa, chitetezo changa ndi mpulumutsi wanga. [3] Mulungu wanga ndiye thanthwe langa, mʼmene ndimathawiramo, chishango changa ndi ndodo yachipulumutso changa. Iye ndi linga langa, pothawirapo panga ndi mpulumutsi wanga. Munandipulumutsa mʼmanja mwa anthu ankhanza. [4] “Ndimayitana Yehova amene ndi woyenera matamando, ndipo ndapulumutsidwa kwa adani anga. [5] “Mafunde a imfa anandizinga; mitsinje yothamanga yachiwonongeko inandiopsa kwambiri. [6] Anandimanga ndi zingwe za ku manda; misampha ya imfa inalimbana nane. [7] “Mʼmasautso anga ndinapemphera kwa Yehova; ndinapemphera kwa Mulungu wanga. Iye ali mʼnyumba yake, anamva mawu anga; kulira kwanga kunafika mʼmakutu ake. [8] “Dziko lapansi linanjenjemera ndi kuchita chivomerezi, maziko a miyamba anagwedezeka; ananjenjemera chifukwa Iye anakwiya. [9] Mʼmphuno mwake munatuluka utsi; moto wonyeketsa unatuluka mʼkamwa mwake, makala amoto anali lawilawi mʼkamwa mwake. [10] Iye anangʼamba thambo natsika pansi; pansi pa mapazi ake panali mitambo yakuda. [11] Iye anakwera pa Kerubi ndi kuwuluka; nawuluka ndi mphepo mwaliwiro. [12] Iye anapanga mdima kukhala chofunda chake, mitambo yakuda ya mlengalenga. [13] Mʼkuwala kumene kunali pamaso pake munkachokera makala amoto alawilawi. [14] Yehova anabangula kumwamba ngati bingu, mawu a Wammwambamwamba anamveka ponseponse. [15] Iye anaponya mivi yake, nabalalitsa adani ake, ndi zingʼaningʼani zake anawagonjetsa. [16] Zigwa za mʼnyanja zinaonekera poyera, ndipo maziko a dziko lapansi anakhala poyera, Yehova atabangula mwaukali, pamene mpweya wamphamvu unatuluka mʼmphuno mwake. [17] “Ali kumwamba, Iye anatambalitsa dzanja lake ndipo anandigwira; anandivuwula mʼmadzi ozama. [18] Anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu, adani anga amene anali amphamvu kuposa ine. [19] Adaniwo analimbana nane pamene ndinali pa mavuto, koma Yehova anali thandizo langa. [20] Iye anandipititsa kumalo otakasuka; anandipulumutsa chifukwa amakondwera nane. [21] “Yehova wandithandiza molingana ndi chilungamo changa; molingana ndi makhalidwe anga abwino, Iye wandipulumutsa. [22] Pakuti ine ndinatsata njira za Yehova; ndilibe mlandu wochoka pamaso pa Mulungu wanga. [23] Malamulo ake onse ali pamaso panga, sindinasiye malangizo ake. [24] Ndakhala moyo wosalakwa pamaso pake ndipo ndakhala ndi kupewa tchimo. [25] Yehova wandipatsa mphotho molingana ndi chilungamo changa, molingana ndi makhalidwe anga abwino pamaso pake. [26] “Kwa wokhulupirika, Inu mumaonetsa kukhulupirika kwanu, kwa anthu amakhalidwe abwino, Inu mumaonetsanso makhalidwe abwino, [27] Kwa woyera mtima, Inu mumaonetsa kuyera mtima kwanu, koma kwa anthu achinyengo mumaonetsanso kunyansidwa nawo. [28] Inu mumapulumutsa anthu odzichepetsa, koma maso anu amatsutsana ndi odzikuza ndipo mumawatsitsa. [29] Inu Yehova, ndinu nyale yanga; Yehova wasandutsa mdima wanga kukhala kuwunika. [30] Ndi thandizo lanu nditha kulimbana ndi gulu la ankhondo, ndi Mulungu wanga nditha kuchita zosatheka ndi munthu. [31] “Kunena za Mulungu, zochita zake ndi zangwiro; mawu a Yehova alibe cholakwika. Iye ndi chishango kwa onse amene amathawira kwa iye. [32] Mulungu wina ndi uti wofanana nanu Yehova? Ndipo ndani amene ndi Thanthwe kupatula Mulungu wathu? [33] Ndi Mulungu amene anandipatsa mphamvu ndi kulungamitsa njira yanga. [34] Iye amasandutsa mapazi anga kukhala ngati ambawala yayikazi; Iye amandithandiza kuyimirira pamwamba pa mapiri. [35] Iye amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo; manja anga amatha kuthyola uta wachitsulo. [36] Inu mundipatsa ine chishango chanu cha chigonjetso; mumawerama kuti mundikweze. [37] Inu mwalimbitsa njira yanga kuti ndiyende bwino, kuti mapazi anga asaterereke. [38] “Ine ndinathamangitsa adani anga ndi kuwakantha; sindinabwerere mpaka iwo atawonongedwa. [39] Ndinawakantha kotheratu, ndipo sanathe kudzukanso; Iwo anagwera pansi pa mapazi anga. [40] Inu munandipatsa ine mphamvu yochitira nkhondo; munagwaditsa adani anga pa mapazi anga. [41] Inu muchititsa kuti adani anga atembenuke ndi kuthawa; ndipo ndinawononga adani anga. [42] Iwo anafuwula kupempha thandizo, koma panalibe ndi mmodzi yemwe owapulumutsa. Analirira kwa Yehova, koma sanawayankhe. [43] Ine ndinawaperesa ngati fumbi la pa dziko lapansi; ndinawasinja ndipo ndinawapondaponda ngati matope a mʼmisewu. [44] “Inu mwandipulumutsa mʼmanja mwa mitundu ya anthu; Inu mwandisunga kuti ndikhale mtsogoleri wa anthu a mitundu ina. Anthu amene sindikuwadziwa ali pansi pa ulamuliro wanga. [45] Alendo amadzipereka okha pamaso panga; akangomva za ine, amandigonjera. [46] Iwo onse anataya mtima; anatuluka mʼmalinga awo akunjenjemera. [47] “Yehova ndi wamoyo! Litamandidwe Thanthwe langa. Akuzike Mulungu, Thanthwe, Mpulumutsi wanga! [48] Iye ndi Mulungu amene amabwezera chilango, amene amayika anthu a mitundu yonse pansi pa ulamuliro wanga, [49] amene amandimasula mʼmanja mwa adani anga. Inu munandikuza kuposa adani anga; munandilanditsa mʼmanja mwa anthu ankhanza. [50] Choncho ine ndidzakutamandani Inu Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina; ndidzayimba nyimbo zotamanda dzina lanu. [51] “Iye amapereka chipambano chachikulu kwa mfumu yake, amaonetsa kukoma mtima kwa wodzozedwa wake, kwa Davide ndi zidzukulu zake kwamuyaya.”
