1 Timoteyo 2:1-15 OCCL

[1] Tsono choyamba ndikukupemphani kuti mupempherere anthu onse. Mapemphero anu akhale opemba, opempha, opempherera ena ndi oyamika. [2] Mupempherere mafumu ndi onse aulamuliro, kuti tikhale moyo wamtendere ndi bata, woopa Mulungu ndi oyera mtima. [3] Izi ndi zabwino ndipo zimakondweretsa Mulungu Mpulumutsi wathu, [4] amene amafuna kuti anthu onse apulumutsidwe ndipo kuti adziwe choonadi. [5] Pakuti pali Mulungu mmodzi yekha ndi Mʼkhalapakati mmodzi yekha pakati pa Mulungu ndi anthu, munthu uja Khristu Yesu. [6] Iyeyu anadzipereka kukhala dipo lowombolera anthu onse. Umenewu ndi umboni umene waperekedwa mu nthawi yake yoyenera. [7] Nʼchifukwa chake anandisankha kukhala mlaliki ndiponso mtumwi wophunzitsa anthu a mitundu ina mawu achikhulupiriro choona. Sindikunama ayi, ndikunena zoona. [8] Choncho ndikufuna kuti paliponse popemphera, amuna azikweza manja awo kwa Mulungu mopanda mkwiyo kapena kukangana. [9] Ndikufunanso kuti amayi azivala mwaulemu, modzilemekeza ndi moyenera. Adzikongoletse koma osati ndi tsitsi loluka mowonjeza muyeso kapena zokongoletsa zagolide kapena mikanda yamtengowapatali kapena ndi zovala zamtengowapatali. [10] Koma adzikongoletse ndi ntchito zabwino zoyenera mayi wopembedza Mulungu. [11] Amayi azikhala chete pophunzitsidwa ndi mtima ogonjera kwathunthu. [12] Ine sindikulola kuti amayi aziphunzitsa kapena kulamulira amuna; koma akhale chete. [13] Pakuti Adamu ndiye anayamba kupangidwa kenaka Hava. [14] Ndipo Adamu si amene ananyengedwa koma mkazi ndiye amene ananyengedwa nachimwa. [15] Ndipo mkazi adzapulumutsidwa pobereka mwana ngati apitiriza kukhala mʼchikhulupiriro, mʼchikondi ndi mʼkuyera mtima pamodzi ndi kudzichepetsa konse.

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app ★★★★★4.8 · 216K ratings Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.