1 Mbiri 8:1-40 OCCL

[1] Benjamini anabereka Bela mwana wake woyamba, wachiwiri Asibeli, wachitatu Ahara, [2] wachinayi Noha ndipo wachisanu Rafa. [3] Ana a Bela anali awa: Adari, Gera, Abihudi, [4] Abisuwa, Naamani, Ahowa, [5] Gera, Sefufani ndi Hiramu. [6] Zidzukulu za Ehudi, zimene zinali atsogoleri a mabanja a amene amakhala ku Geba ndipo zinasamutsidwa kupita ku Manahati zinali izi: [7] Naamani, Ahiya ndi Gera, amene anawasamutsa ndipo anabereka Uza ndi Ahihudi. [8] Saharaimu anabereka ana ku Mowabu atalekana ndi akazi ake, Husimu ndi Baara. [9] Mwa mkazi wake Hodesi anabereka Yobabu, Zibiya, Mesa, Malikamu, [10] Yeusi, Sakiya ndi Mirima. Awa ndiye ana ake, atsogoleri a mabanja awo. [11] Mwa mkazi wake Husimu anabereka Abitubi ndi Elipaala. [12] Ana a Elipaala anali awa: Eberi, Misamu, Semedi (amene anamanga mizinda ya Ono ndi Lodi ndi midzi yake yozungulira) [13] ndiponso Beriya ndi Sema, amene anali atsogoleri a mabanja a amene ankakhala ku Ayaloni ndipo anathamangitsa nzika za ku Gati. [14] Ahiyo, Sasaki, Yeremoti, [15] Zebadiya, Aradi, Ederi, [16] Mikayeli, Isipa ndi Yoha anali ana a Beriya. [17] Zebadiya, Mesulamu, Hiziki, Heberi, [18] Isimerai, Iziliya ndi Yobabu anali ana a Elipaala. [19] Yakimu, Zikiri, Zabidi, [20] Elienai, Ziletai, Elieli, [21] Adaya, Beraya ndi Simirati anali ana a Simei. [22] Isipani, Eberi, Elieli, [23] Abidoni, Zikiri, Hanani, [24] Hananiya, Elamu, Anitotiya, [25] Ifideya ndi Penueli anali ana a Sasaki. [26] Samuserai, Sehariya, Ataliya, [27] Yaaresiya, Eliya ndi Zikiri anali ana a Yerohamu. [28] Onsewa anali atsogoleri a mabanja, anthu otchuka potsata mibado yawo, ndipo ankakhala mu Yerusalemu. [29] Yeiyeli amene amabereka Gibiyoni ankakhala ku Gibiyoni. Dzina la mkazi wake linali Maaka, [30] ndipo mwana wake woyamba anali Abidoni, motsatana ndi Zuri, Kisi, Baala, Neri, Nadabu, [31] Gedori, Ahiyo, Zekeri [32] ndi Mikiloti, amene anabereka Simea. Iwowa ankakhalanso ku Yerusalemu ndi abale awo. [33] Neri anabereka Kisi. Kisi anabereka Sauli, ndipo Sauli anabereka Yonatani, Maliki-Suwa, Abinadabu ndi Esibaala. [34] Mwana wa Yonatani anali Meri-Baala, amene anabereka Mika. [35] Ana a Mika anali awa: Pitoni, Meleki, Tareya ndi Ahazi. [36] Ahazi anabereka Yehoyada, Yehoyada anabereka Alemeti, Azimaveti ndi Zimuri, ndipo Zimuri anabereka Moza. [37] Moza anabereka Bineya. Ana ake anali Rafa, Eleasa ndi Azeli. [38] Azeli anali ndi ana asanu ndi mmodzi, ndipo mayina awo anali awa: Azirikamu, Bokeru, Ismaeli, Seariya, Obadiya ndi Hanani. Onsewa anali ana a Azeli. [39] Ana a Eseki mʼbale wake anali awa: Mwana wake woyamba Ulamu, wachiwiri Yeusi ndipo wachitatu Elifeleti. [40] Ana a Ulamu anali asilikali olimba mtima amene amadziwa kugwiritsa ntchito uta. Iwo anali ndi ana ndi adzukulu ambiri ndipo onse analipo 150. Onsewa anali adzukulu a Benjamini.

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.